1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe,
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife;
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa;
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu,
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu;
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu,
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza;
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita;
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha;
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija:
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja,
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu;
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu,
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka,
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala”