1 Yehova ndinu Mulungu wanga;
2 Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.
3 Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;
4 Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,
5 ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.
6 Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera
7 Iye adzachotsa kulira
8 Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,
9 Tsiku limenelo iwo adzati,
10 Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;
11 Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,
12 Iye adzagumula malinga awo ataliatali