1 Uthenga wonena za Turo:
2 Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja,
3 Pa nyanja zazikulu
4 Chita manyazi, iwe Sidimu
5 Mawuwa akadzamveka ku Igupto,
6 Wolokerani ku Tarisisi,
7 Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja,
8 Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina,
9 Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi
10 Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo
11 Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja
12 Iye anati, “Simudzakondwanso konse,
13 Onani dziko la Ababuloni,
14 Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi;
15 Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 “Tenga zeze wako uzungulire mzinda,
17 Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
18 Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.