1 Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya:
2 Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya,
3 Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi;
4 Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga;
5 Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione
6 Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta
7 Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta,
8 zonse zoteteza Yuda zachotsedwa.
9 inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide
10 Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu
11 Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime
12 Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse
13 Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala;
14 Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti,
16 Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo
17 “Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba
18 Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira
19 Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako
20 “Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 “Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’ ” Yehova wayankhula chomwechi.