Isaías 10

NYA

1 Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo,

2 kuwalanda anthu osauka ufulu wawo

3 Kodi mudzatani pa tsiku la chilango,

4 Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa

5 “Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga,

6 Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu,

7 Koma izi si zimene akufuna kukachita,

8 Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’

9 ‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi?

10 Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano,

11 nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake

12 Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.

13 Pakuti mfumuyo ikuti,

14 Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu

15 Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito,

16 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse

17 Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto,

18 Ankhondo ake adzawonongedwa

19 Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri,

20 Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli,

21 Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo

22 Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja,

23 Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse

24 Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti,

25 Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu

26 Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu,

27 Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu,

28 Adani alowa mu Ayati

29 Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti,

30 Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu!

31 Anthu a ku Madimena akuthawa;

32 Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu;

33 Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,

34 Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira;

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado