1 Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,
2 Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;
3 Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,
4 Iwo alibe zosautsa;
5 Saona mavuto monga anthu ena;
6 Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;
7 Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;
8 Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;
9 Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba
10 Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo
11 Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?
12 Umu ndi mmene oyipa alili;
13 Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;
14 Tsiku lonse ndapeza mavuto;
15 Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”
16 Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,
17 kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;
18 Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;
19 Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,
20 Monga loto pamene wina adzuka,
21 Pamene mtima wanga unasautsidwa
22 ndinali wopusa ndi wosadziwa;
23 Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;
24 Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu
25 Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?
26 Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,
27 Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;
28 Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.