Salmos 119

NYA

1 Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,

2 Odala ndi amene amasunga malamulo ake,

3 Sachita cholakwa chilichonse;

4 Inu mwapereka malangizo

5 Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika

6 Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,

7 Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,

8 Ndidzamvera zophunzitsa zanu;

9 Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?

10 Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;

11 Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga

12 Mutamandike Inu Yehova;

13 Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse

14 Ndimakondwera potsatira malamulo anu

15 Ndimalingalira malangizo anu

16 Ndimakondwera ndi malamulo anu;

17 Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;

18 Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona

19 Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;

20 Moyo wanga wafowoka polakalaka

21 Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,

22 Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo

23 Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,

24 Malamulo anu amandikondweretsa;

25 Moyo wanga wakangamira fumbi;

26 Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;

27 Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;

28 Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;

29 Mundichotse mʼnjira zachinyengo;

30 Ndasankha njira ya choonadi;

31 Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;

32 Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,

33 Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;

34 Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu

35 Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,

36 Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,

37 Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;

38 Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,

39 Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,

40 Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!

41 Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,

42 ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,

43 Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,

44 Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,

45 Ndidzayendayenda mwaufulu,

46 Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu

47 popeza ndimakondwera ndi malamulo anu

48 Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,

49 Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,

50 Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:

51 Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,

52 Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,

53 Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa

54 Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga

55 Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,

56 Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:

57 Yehova, Inu ndiye gawo langa;

58 Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;

59 Ndinalingalira za njira zanga

60 Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza

61 Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,

62 Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu

63 Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,

64 Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,

65 Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu

66 Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,

67 Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,

68 Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;

69 Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,

70 Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,

71 Ndi bwino kuti ndinasautsidwa

72 Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri

73 Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;

74 Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,

75 Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama

76 Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,

77 Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,

78 Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;

79 Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,

80 Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu

81 Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,

82 Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;

83 Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi

84 Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?

85 Anthu osalabadira za Mulungu,

86 Malamulo anu onse ndi odalirika;

87 Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi

88 Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,

89 Mawu anu Yehova ndi amuyaya;

90 Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;

91 Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,

92 Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,

93 Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,

94 Ndine wanu, ndipulumutseni;

95 Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,

96 Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,

97 Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!

98 Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,

99 Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse

100 Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,

101 Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa

102 Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,

103 Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,

104 Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;

105 Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga

106 Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,

107 Ndazunzika kwambiri;

108 Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,

109 Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,

110 Anthu oyipa anditchera msampha,

111 Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;

112 Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu

113 Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,

114 Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;

115 Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,

116 Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;

117 Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;

118 Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,

119 Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;

120 Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;

121 Ndachita zolungama ndi zabwino;

122 Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,

123 Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,

124 Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,

125 Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,

126 Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;

127 Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu

128 ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,

129 Maumboni anu ndi odabwitsa

130 Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;

131 Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,

132 Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,

133 Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;

134 Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,

135 Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu

136 Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,

137 Yehova ndinu wolungama,

138 Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;

139 Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga

140 Mawu anu ndi woyera kwambiri

141 Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,

142 Chilungamo chanu nʼchamuyaya,

143 Mavuto ndi masautso zandigwera,

144 Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;

145 Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,

146 Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni

147 Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;

148 Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,

149 Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;

150 Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,

151 Koma Inu Yehova muli pafupi,

152 Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu

153 Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,

154 Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;

155 Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,

156 Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;

157 Adani amene akundizunza ndi ambiri,

158 Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,

159 Onani momwe ndimakondera malangizo anu;

160 Mawu anu onse ndi owona;

161 Olamulira amandizunza popanda chifukwa,

162 Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,

163 Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,

164 Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku

165 Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,

166 Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,

167 Ndimamvera umboni wanu

168 Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,

169 Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;

170 Kupempha kwanga kufike pamaso panu;

171 Matamando asefukire pa milomo yanga,

172 Lilime langa liyimbe mawu anu,

173 Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza

174 Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,

175 Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,

176 Ndasochera ngati nkhosa yotayika,

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado