Números 2

NYA vs NTLH

Sair da comparação
NTLH Nova Tradução na Linguagem de Hoje 2000
1 Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni:
1 O Senhor Deus disse a Moisés e a Arão o seguinte:
2 “Aisraeli azimanga misasa yawo mozungulira tenti ya msonkhano motalikira pangʼono. Munthu aliyense amange pamene pali mbendera ya fuko lake.”
2 — Quando os israelitas armarem o acampamento, cada um ficará perto da bandeira do seu grupo e do estandarte do seu grupo de famílias. Eles acamparão em volta da Tenda Sagrada e de frente para ela.
3 Kummawa, kotulukira dzuwa, magulu a msasa wa Yuda amange pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Ayudawo ndi Naasoni mwana wa Aminadabu.
3 — ausente —
4 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 74,600.
4 — ausente —
5 Fuko la Isakara lidzamanga pafupi ndi Yuda. Mtsogoleri wa gulu la Isakara ndi Netanieli mwana wa Zuwara.
5 — ausente —
6 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 54,400.
6 — ausente —
7 Lotsatira lidzakhala fuko la Zebuloni. Mtsogoleri wa gulu la Zebuloni ndi Eliabu mwana wa Heloni.
7 — ausente —
8 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 57,400.
8 — ausente —
9 Anthu onse aamuna mʼmisasa ya Yuda, chiwerengero chawo ndi 186,400 monga mwa magulu awo. Iwowo ndiwo aziyamba kusamuka.
9 O grupo de Judá, num total de cento e oitenta e seis mil e quatrocentos homens, marchará primeiro.
10 Kummwera kudzakhala magulu a msasa wa Rubeni pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu la Rubeni ndi Elizuri mwana wa Sedeuri.
10 — ausente —
11 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 46,500.
11 — ausente —
12 Fuko la Simeoni lidzamanga pafupi ndi Rubeni. Mtsogoleri wa gulu la Simeoni ndi Selumieli mwana wa Zurisadai.
12 — ausente —
13 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 59,300.
13 — ausente —
14 Lotsatira lidzakhala fuko la Gadi. Mtsogoleri wa gulu la Gadi ndi Eliyasafu mwana wa Deuweli.
14 — ausente —
15 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 45,650.
15 — ausente —
16 Anthu onse aamuna mu msasa wa Rubeni, chiwerengero chawo monga mwa magulu awo, ndi 151,450. Iwowo azikhala achiwiri posamuka.
16 O grupo de Rúben, num total de cento e cinquenta e um mil quatrocentos e cinquenta homens, marchará em segundo lugar.
17 Tsono tenti ya msonkhano ndi msasa wa Alevi zidzakhala pakati pa misasayo. Iwo adzasamuka monga momwe anamangira misasa yawo, aliyense pa malo ake pamene pali mbendera yake.
17 — Entre os primeiros dois grupos e os dois últimos, marcharão os levitas , levando a Tenda. Os grupos marcharão na mesma ordem em que acamparem, cada um no seu lugar, seguindo a sua bandeira.
18 Kumadzulo kudzakhala magulu a msasa wa Efereimu pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Aefereimuwo ndi Elisama mwana wa Amihudi.
18 — ausente —
19 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 40,500.
19 — ausente —
20 Fuko la Manase lidzakhala pafupi ndi Efereimu. Mtsogoleri wa Amanase ndi Gamalieli mwana wa Pedazuri.
20 — ausente —
21 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 32,200.
21 — ausente —
22 Lotsatira lidzakhala fuko la Benjamini. Mtsogoleri wa Abenjamini ndi Abidani mwana wa Gideoni.
22 — ausente —
23 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 35,400.
23 — ausente —
24 Anthu onse aamuna mu msasa wa Efereimu, chiwerengero chawo ndi 108,100 monga mwa magulu awo. Iwowo azikhala achitatu posamuka.
24 O grupo de Efraim, num total de cento e oito mil e cem homens, marchará em terceiro lugar.
25 Kumpoto kudzakhala msasa wa magulu a Dani pamene pali mbendera yawo. Mtsogoleri wa Adani ndi Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
25 — ausente —
26 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 62,700.
26 — ausente —
27 Fuko la Aseri lidzamanga pafupi ndi iwowo. Mtsogoleri wa Aaseri ndi Pagieli mwana wa Okirani.
27 — ausente —
28 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 41,500.
28 — ausente —
29 Lotsatira lidzakhala fuko la Nafutali. Mtsogoleri wa Anafutali ndi Ahira mwana wa Enani.
29 — ausente —
30 Chiwerengero cha gulu lake lankhondo ndi 53,400.
30 — ausente —
31 Anthu onse aamuna mu msasa wa Dani chiwerengero chawo ndi 157,600. Iwo azidzanyamuka pomaliza, ndi mbendera zawo.
31 O grupo de Dã, num total de cento e cinquenta e sete mil e seiscentos homens, marchará por último.
32 Amenewa ndi Aisraeli monga mwa mabanja a makolo awo. Chiwerengero cha Aisraeli onse mʼmisasa chinali 603,550, mwa magulu awo.
32 O número total dos homens de Israel registrados nos exércitos, grupo por grupo, foi de seiscentos e três mil quinhentos e cinquenta.
33 Koma Alevi sanawawerenge pamodzi ndi Aisraeli enawo monga momwe Yehova analamulira Mose.
33 Como o Senhor havia ordenado a Moisés, os levitas não foram contados com os outros israelitas.
34 Choncho Aisraeli anachita zonse zomwe Yehova analamulira Mose. Umo ndi momwe amamangira misasa yawo pamene panali mbendera zawo, ndipo ankasamuka monga mwa mafuko a makolo awo.
34 Assim, o povo de Israel fez tudo como o Senhor havia ordenado a Moisés. Eles acamparam, cada grupo debaixo da sua própria bandeira, e cada israelita começou a marchar com o seu grupo de famílias.

Ler em outra tradução

Comparar com outra