1 Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;
2 Apereka cholowa chathu kwa obwera,
3 Takhala amasiye ndi wopanda abambo,
4 Tiyenera kugula madzi amene timamwa,
5 Otilondola atigwira pakhosi;
6 Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya
7 Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,
8 Akapolo akutilamulira,
9 Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe
10 Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,
11 Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,
12 Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,
13 Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;
14 Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;
15 Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;
16 Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.
17 Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,
18 pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,
19 Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;
20 Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?
21 Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;
22 pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,