1 Yehova akuti,
2 Ndidzatuma alendo ku Babuloni
3 Okoka uta musawalekerere
4 Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni
5 Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye
6 “Thawaniko ku Babuloni!
7 Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova;
8 Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka.
9 Ena anati, “ ‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni,
10 “ ‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa;
11 “Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi,
12 Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni!
13 Inu muli ndi mitsinje yambiri
14 Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti:
15 “Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake;
16 Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba.
17 “Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru;
18 Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo.
19 Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo.
20 “Iwe Babuloni ndi ndodo yanga,
21 ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo,
22 Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi,
23 Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto,
24 “Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
25 “Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga,
26 Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga
27 “Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko!
28 Konzekeretsani mitundu ya anthu.
29 Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira,
30 Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo;
31 Othamanga akungopezanapezana,
32 Madooko onse alandidwa,
33 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,
34 A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga,
35 Anthu a ku Ziyoni anene kuti,
36 Nʼchifukwa chake Yehova akuti,
37 Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka,
38 Anthu ake onse adzabangula ngati mkango,
39 Ngati achita dyera
40 “Ine ndidzawatenga
41 “Ndithu Babuloni walandidwa,
42 Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni;
43 Mizinda yake yasanduka bwinja,
44 Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni,
45 “Tulukani mʼBabuloni anthu anga!
46 Musataye mtima kapena kuchita mantha
47 Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu
48 Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo
49 “Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi.
50 Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni,
51 Inu mukuti, “Tikuchita manyazi,
52 Nʼchifukwa chake Yehova akuti,
53 Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga
54 “Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni.
55 Pakuti Yehova akuwononga Babuloni,
56 Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni,
57 Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake,
58 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
59 Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
60 Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
61 Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
62 Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63 Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
64 Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’ ”