1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
2 Yehova akuti,
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati,
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli;
5 Mudzalimanso minda ya mpesa
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula
7 Yehova akuti,
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto,
9 Adzabwera akulira;
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina;
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni;
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino,
15 Yehova akuti,
16 Yehova akuti,
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,”
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti,
19 Popeza tatembenuka mtima,
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa,
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu;
22 Udzakhala jenkha mpaka liti,
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti,
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova,
32 Silidzakhala ngati pangano
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake,
35 Yehova akuti,
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
37 Yehova akuti,
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”