1 Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 Ndipo Yobu anati:
3 “Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe
4 Tsiku limenelo lisanduke mdima;
5 Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;
6 Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;
7 Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;
8 Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,
9 Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga
11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,
20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,
22 amene amakondwa ndi kusangalala
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera;
26 Ndilibe mtendere kapena bata,