Isaías 66

NYA

1 Yehova akuti,

2 Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi,

3 Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna

4 Inenso ndawasankhira chilango chowawa

5 Imvani mawu a Yehova,

6 Imvani mfuwu mu mzinda,

7 “Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa

8 Ndani anamvapo zinthu zoterezi?

9 Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira,

10 “Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye,

11 Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake

12 Yehova akuti,

13 Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo,

14 Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu.

15 Taonani, Yehova akubwera ngati moto,

16 Pakuti Yehova adzalanga anthu onse

17 Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”

18 “Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.

19 “Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.

20 Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.

21 Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.

22 “Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.

23 “Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.

24 “Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado