1 Yehova anandiyankhula kuti:
2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo.
3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti,
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja;
5 Anakupanga ndi matabwa
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako,
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako.
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako,
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari.
19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda.
24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali
26 Anthu opalasa ako amakupititsa
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako,
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi,
30 Iwo akufuwula,
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe
32 Akuyimba nyimbo
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja,
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola.