1 Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;
2 Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula
3 Ndidzalalikira dzina la Yehova.
4 Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,
5 Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,
6 Kodi mukumubwezera Yehova chotere,
7 Kumbukirani masiku amakedzana;
8 Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,
9 Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,
10 Anamupeza mʼchipululu,
11 ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake
12 Yehova yekha ndiye anamutsogolera;
13 Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko
14 pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,
15 Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;
16 Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo
17 Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,
18 Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;
19 Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana
20 Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga,
21 Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu
22 Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto,
23 “Ndidzawawunjikira masautso
24 Ndidzawatumizira njala yoopsa,
25 Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana;
26 Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza
27 koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze,
28 Iwo ndi mtundu wopanda maganizo,
29 Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi
30 Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000
31 Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,
32 Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu
33 Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka,
34 “Kodi zimenezi sindinazisunge
35 Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.
36 Yehova adzaweruza anthu ake
37 Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo,
38 milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo
39 “Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo!
40 Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,
41 pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira
42 Mivi yanga idzakhuta magazi awo
43 Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,
44 Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
45 Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
46 iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
47 Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
48 Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
49 “Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
50 Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
51 Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
52 Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”