1 Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola
2 Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino
3 Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,
4 Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.
5 Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.
6 Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,
7 Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,
8 Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;
9 ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.
10 Wokondedwayo ine ndine wake,
11 Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,
12 Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,
13 Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,