1 Tsoka kwa amene simukulabadira kanthu ku Ziyoni,
2 Pitani ku mzinda wa Kaline mukawuyangʼane;
3 Inu simulabadirako kuti tsiku loyipa lidzafika,
4 Mumagona pa mabedi owakongoletsa ndi minyanga ya njovu,
5 Mumayimba azeze anu ndi kumangopeka
6 Mumamwera vinyo mʼzipanda zodzaza
7 Nʼchifukwa chake inu mudzakhala mʼgulu la anthu oyamba kupita ku ukapolo;
8 Ambuye Yehova walumbira mʼdzina lake. Yehova Mulungu Wamphamvuzonse walengeza kuti,
9 Ngati anthu khumi otsala adzabisala mʼnyumba imodzi, nawonso adzafa ndithu.
10 Ndipo ngati mʼbale wake wa wina wakufayo, woyenera kusamala za maliro, adzafika kudzatulutsa mitembo mʼnyumbamo nʼkufunsa aliyense amene akubisalabe mʼnyumbamo kuti, “Kodi uli ndi wina wamoyo mʼmenemo?” Ndipo munthu wobisalayo ndi kuyankha kuti, “Ayi,” mʼbaleyo adzanena kuti, “Khala chete! Ife tisayerekeze kutchula dzina la Yehova.”
11 Pakuti Yehova walamula kuti
12 Kodi akavalo amathamanga pa thanthwe?
13 Inu amene mukunyadira kuti munagonjetsa Lo Debara
14 Koma Yehova Mulungu Wamphamvuzonse akulengeza kuti,