2 Tessalonicenses 3

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs BKJ

Sair da comparação
1 Potsiriza, abale, mutipempherere kuti uthenga wa Ambuye ufalikire msanga ndi kulemekezedwa monga momwe munachitira inu.
1 E, finalmente, irmãos, orai por nós, para que a palavra do Senhor tenha livre curso e seja glorificada, como também o é entre vós.
2 Ndipo pempherani kuti tilanditsidwe mʼmanja mwa anthu ovuta ndi oyipa, pakuti si onse amene ali nacho chikhulupiriro.
2 E para que sejamos livres de homens irracionais e maus; porque nem todos os homens possuem a fé.
3 Koma Ambuye ndi wokhulupirika, ndipo adzakulimbikitsani ndi kukutetezani kwa woyipayo.
3 Mas o Senhor é fiel, e vos confirmará e vos guardará do maligno.
4 Tili ndi chikhulupiriro mwa Ambuye kuti mukuchita zonse ndipo mudzapitirira kuchita zimene tinakulamulirani.
4 E confiamos quanto a vós no Senhor, que não só fazeis como fareis as coisas que vos mandamos.
5 Ambuye atsogolere mitima yanu kuti mudziwe chikondi cha Mulungu ndiponso kupirira kumene Khristu amapereka.
5 E o Senhor encaminhe os vossos corações no amor de Deus e na paciente espera por Cristo.
6 Abale, tikukulamulani mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, kuti mupewe mʼbale aliyense amene ndi waulesi ndi wachisokonezo, wosafuna kutsata zimene tinakuphunzitsani.
6 Nós vos mandamos, irmãos, em nome de nosso Senhor Jesus Cristo, que vos aparteis de todo irmão que anda desordenadamente e não segundo a tradição que ele recebeu de nós.
7 Pakuti inu mukudziwa zimene muyenera kuchita pofuna kutitsatira. Ife sitinali alesi pamene tinali nanu
7 Porque vós mesmos sabeis como convém seguir-nos, pois que não nos portamos desordenadamente entre vós,
8 ndipo sitinadye chakudya cha aliyense osalipira. Komatu tinkagwira ntchito mwamphamvu usiku ndi usana kuti tisakhale cholemetsa kwa aliyense.
8 nem comemos o pão de homem algum de graça, mas com trabalho e fadiga, trabalhando noite e dia, para não sermos pesados a nenhum de vós.
9 Sitinachite zimenezi chifukwa choti tinalibe mphamvu zolamula kuti mutithandize koma kuti tikhale chitsanzo choti mutsatire.
9 Não porque não tivéssemos tal direito, mas para vos dar em nós mesmos exemplo, para nos seguirdes.
10 Pakuti ngakhale pamene tinali nanu, tinakupatsani lamulo lakuti, “Munthu wosafuna kugwira ntchito, asadye.”
10 Porque, quando ainda estávamos convosco, isto vos mandamos: que, se alguém não quiser trabalhar, também não coma.
11 Ife tikumva kuti pakati panu pali ena amene ndi alesi. Iwo safuna kugwira ntchito, koma amangolowerera pa za eni.
11 Porquanto ouvimos que há alguns entre vós que andam desordenadamente, não trabalhando, mas são intrometidos.
12 Mʼdzina la Ambuye Yesu Khristu, tikuwalamula ndi kuwakakamiza kuti azigwira ntchito mwabata ndi kumadya chakudya chodzigwirira ntchito okha.
12 A esses tais, porém, mandamos e exortamos, por nosso Senhor Jesus Cristo, que, trabalhando com sossego, comam o seu próprio pão.
13 Koma inu abale, musatope nʼkuchita zabwino.
13 Mas vós, irmãos, não vos canseis de fazer o bem.
14 Ngati wina aliyense akana kumvera malangizo athu a mʼkalatayi, mumuonetsetse ameneyo ndipo musayanjane naye kuti achite manyazi.
14 Mas, se algum homem não obedecer à nossa palavra por esta carta, notai tal homem, e não vos mistureis com ele, para que se envergonhe.
15 Komatu musamutenge kukhala mdani, koma muchenjezeni ngati mʼbale.
15 Todavia, não o considere como inimigo, mas admoestai-o como um irmão.
16 Tsopano Ambuye mwini mtendere akupatseni mtendere nthawi zonse mwa njira iliyonse. Ambuye akhale ndi inu nonse.
16 Ora, o próprio Senhor da paz vos conceda a paz sempre, por todos os meios. O Senhor seja com todos vós.
17 Ine Paulo, ndikulemba malonje awa ndi dzanja langa, chimene ndi chizindikiro chodziwika mʼmakalata anga onse. Umo ndi mmene ndimalembera.
17 Saudação de Paulo, com minha própria mão, que é o sinal em todas as cartas; assim escrevo.
18 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale ndi inu nonse.
18 A graça de nosso Senhor Jesus Cristo seja com todos vós. Amém.

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar 2 Tessalonicenses 3, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.