1 Ana a Levi anali awa:
2 Ana a Kohati anali awa:
3 Ana a Amramu anali awa:
4 Eliezara anabereka Finehasi,
5 Abisuwa anabereka Buki,
6 Uzi anabereka Zerahiya,
7 Merayoti anabereka Amariya,
8 Ahitubi anabereka Zadoki,
9 Ahimaazi anabereka Azariya,
10 Yohanani anabereka Azariya (uyu ndi amene anatumikira monga wansembe mʼNyumba ya Mulungu imene Solomoni anamanga mu Yerusalemu),
11 Azariya anabereka Amariya,
12 Ahitubi anabereka Zadoki,
13 Salumu anabereka Hilikiya,
14 Azariya anabereka Seraya,
15 Yehozadaki anagwidwa ukapolo pamene Yehova analola Nebukadinezara kuti agwire ukapolo Yuda ndi Yerusalemu.
16 Ana a Levi anali awa:
17 Mayina a ana a Geresomu ndi awa:
18 Ana a Kohati anali awa:
19 Ana a Merari anali awa:
20 Ana a Geresomu ndi awa:
21 Yowa,
22 Zidzukulu za Kohati ndi izi:
23 Elikana,
24 Tahati, Urieli,
25 Zidzukulu za Elikana ndi izi:
26 Elikana, Zofai,
27 Eliabu,
28 Ana a Samueli ndi awa:
29 Zidzukulu za Merari ndi izi:
30 Simea, Hagiya
31 Awa ndi anthu amene Davide anawayika kuti aziyangʼanira mayimbidwe mʼNyumba ya Yehova, Bokosi la Chipangano litabwera kudzakhala mʼmenemo.
32 Iwo ankatumikira akuyimba nyimbo pa khomo la malo opatulika, tenti ya msonkhano, mpaka Solomoni atamanga Nyumba ya Yehova mu Yerusalemu. Iwo ankagwira ntchito zawo potsata malamulo amene anawapatsa.
33 Mayina a anthuwo, pamodzi ndi ana awo, anali awa:
34 mwana wa Elikana, mwana wa Yerohamu,
35 mwana wa Zufi, mwana wa Elikana,
36 mwana wa Elikana, mwana wa Yoweli,
37 mwana wa Tahati, mwana wa Asiri,
38 mwana wa Izihari, mwana wa Kohati,
39 ndi Asafu mʼbale wake, amene ankatumikira ku dzanja lake lamanja:
40 mwana wa Mikayeli, mwana wa Baaseya,
41 mwana wa Etini,
42 mwana wa Etani, mwana wa Zima,
43 mwana wa Yahati,
44 ndipo abale awo ena anali a banja la Merari amene amatumikira ku dzanja lake lamanzere:
45 mwana wa Hasabiya,
46 mwana wa Amizi, mwana wa Bani,
47 mwana wa Mahili,
48 Abale awo Alevi anapatsidwa ntchito zina zonse ku malo opatulika ku nyumba ya Mulungu.
49 Koma Aaroni ndi zidzukulu zake anali amene amapereka nsembe pa guwa lansembe zopsereza ndi pa guwa lansembe zofukiza pamodzi ndi zonse zimene zimachitika ku malo opatulika kwambiri, kuchita mwambo wopepesera Israeli, potsata zonse zimene Mose mtumiki wa Mulungu anawalamulira.
50 Ana a Aaroni ndi zidzukulu zake anali awa:
51 Buki,
52 Merayoti, Amariya,
53 Zadoki
54 Malo amene iwo anapatsidwa kuti likhale dziko lawo ndi awa: (Malowa anapatsidwa kwa zidzukulu za Aaroni zimene zinali za banja la Kohati, chifukwa malo oyamba kugawidwa anali awo).
55 Iwo anapatsidwa Hebroni mʼdziko la Yuda ndi madera odyetsera ziweto ozungulira malowa.
56 Koma minda ndi midzi yozungulira mzindawo zinapatsidwa kwa Kalebe mwana wa Yefune.
57 Kotero zidzukulu za Aaroni zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako), ndi Libina, Yatiri, Esitemowa,
58 Hileni, Debri,
59 Asani, Yuta ndi Beti-Semesi pamodzi ndi madera odyetsera ziweto ozungulira malowa.
60 Ndipo ku fuko la Benjamini anapatsidwa Gibiyoni, Geba, Alemeti ndi Anatoti, pamodzi ndi madera odyetsera ziweto ozungulira malowa.
61 Zidzukulu zotsala za Kohati anazigawira midzi khumi kuchokera ku mabanja a fuko la theka la Manase.
62 Zidzukulu za Geresomu banja ndi banja zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Isakara, Aseri ndi Nafutali, ndi gawo lina la fuko la Manase limene lili ku Basani.
63 Zidzukulu za Merari banja ndi banja zinapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
64 Kotero Aisraeli anapatsa Alevi mizindayi ndi madera a msipu ozungulira malowa.
65 Kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini anawapatsa mizinda imene inawatchula kale mayina.
66 Mabanja ena a Kohati anapatsidwanso malo kuchokera ku fuko la Efereimu.
67 Kuchokera ku dziko lamapiri la Efereimu anapatsidwa Sekemu (mzinda wopulumukirako) ndi Gezeri,
68 Yokineamu, Beti-Horoni,
69 Ayaloni ndi Gati-Rimoni, pamodzi ndi madera odyetsera ziweto ozungulira.
70 Ndipo kuchokera ku theka la fuko la Manase, Aisraeli anapereka Aneri ndi Bileamu pamodzi ndi madera odyetsera ziweto kwa mabanja ena onse a Kohati.
71 Ageresomu analandira malo awa:
72 Kuchokera ku fuko la Isakara
73 Ramoti ndi Anemu, pamodzi ndi malo ake odyetsera ziweto;
74 kuchokera ku fuko la Aseri
75 Hukoki ndi Rehobu, pamodzi ndi malo ake odyetsera ziweto;
76 ndipo kuchokera ku fuko la Nafutali
77 Amerari (Alevi ena onse) analandira madera awa:
78 Kuchokera ku fuko la Rubeni kutsidya kwa Yorodani, kummawa kwa Yeriko,
79 Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo ake odyetsera ziweto;
80 ndipo kuchokera ku fuko la Gadi
81 Hesiboni ndi Yazeri, pamodzi ndi malo ake odyetsera ziweto.