1 Magulu a ana a Aaroni anali awa:
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu,
8 achitatu anagwera Harimu,
9 achisanu anagwera Malikiya,
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi,
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa,
12 a 11 anagwera Eliyasibu,
13 a 13 anagwera Hupa,
14 a 15 anagwera Biliga,
15 a 17 anagwera Heziri,
16 a 19 anagwera Petahiya,
17 a 21 anagwera Yakini,
18 a 23 anagwera Delaya,
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi:
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake:
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti;
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Mwana wa Uzieli: Mika;
25 Mʼbale wa Mika: Isiya;
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi.
27 Ana a Merari:
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Kuchokera kwa Kisi:
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.