1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo,
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,
9 Musanditaye pamene ndakalamba;
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya;
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga
22 Ndidzakutamandani ndi zeze
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo