1 Tamandani Yehova.
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu
11 Sihoni mfumu ya Aamori,
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya,
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa,
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide,
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula
17 makutu ali nawo, koma sakumva
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo,
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova;
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova;
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni,