1 Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu.
2 Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye
3 ndipo ananena uthenga wake:
4 uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,
5 “Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo,
6 “Monga zigwa zotambalala,
7 Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake;
8 “Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto
9 Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi,
10 Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka.
11 Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”
12 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine,
13 kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena?
14 Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
15 Ndipo iye ananena uthenga wake nati,
16 Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu,
17 “Ndikumuona iye koma osati tsopano;
18 Edomu adzagonjetsedwa;
19 Wolamulira adzachokera mwa Yakobo
20 Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu:
21 Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake,
22 komabe inu Akeni mudzawonongedwa,
23 Ndipo ananenanso uthenga wina kuti,
24 Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu;
25 Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.