1 Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
2 Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
3 Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
4 Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
5 Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
6 Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’ ”
7 Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi;
8 Nthawi iliyonse ndikamayankhula,
9 Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye
10 Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti,
11 Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama
13 Imbirani Yehova!
14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa!
15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga
16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene
17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba,
18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni