1 Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse
2 Inu munawadzala ndipo anamera mizu;
3 Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa;
4 Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti
5 Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu
6 Ngakhale abale ako
7 “Ine ndawasiya anthu anga;
8 Anthu amene ndinawasankha
9 Anthu anga amene ndinawasankha
10 Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa,
11 Unawusandutsadi chipululu.
12 Anthu onse owononga abalalikira
13 Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga;
14 “Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.