Gênesis 49

NYA

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;

3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;

4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,

5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,

6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,

7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi

8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;

9 Yuda ali ngati mwana wa mkango;

10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,

11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,

12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,

13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;

14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu

15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira

16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake

17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,

18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,

20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,

21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi

22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,

23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;

24 Koma uta wake sunagwedezeke,

25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;

26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa

27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;

28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.

30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.

31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.

32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado