Ezequiel 30

NYA

1 Yehova anandiyankhula kuti:

2 “Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

3 Pakuti tsiku layandikira,

4 Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

5 Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

7 “ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

8 Nditatha kutentha Igupto

9 “ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

11 Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

12 Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

13 “ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

14 Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

15 Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

16 Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

17 Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

18 Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

19 Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

20 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:

21 “Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.

22 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.

23 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.

24 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.

25 Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.

26 Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado