Êxodo 15

NYA

1 Ndipo Mose ndi Aisraeli anayimbira Yehova nyimbo iyi:

2 Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

3 Yehova ndi wankhondo;

4 Magaleta a Farao ndi asilikali ake ankhondo

5 Nyanja yakuya inawaphimba;

6 Yehova, dzanja lanu lamanja

7 Ndi ulemerero wanu waukulu,

8 Ndi mpweya wotuluka mʼmphuno mwanu

9 Mdaniyo anati,

10 Koma Inu munawuzira mphepo yanu,

11 Ndithu Yehova, pakati pa milungu,

12 Munatambasula dzanja lanu lamanja

13 Ndi chikondi chanu chosasinthika mudzatsogolera

14 Anthu amitundu ina anamva za mbiriyi ndipo ananjenjemera ndi mantha,

15 Tsopano mafumu a ku Edomu agwidwa ndi mantha aakulu,

16 Onse agwidwa ndi mantha woopsa.

17 Inu mudzawalowetsa ndi kuwakhazikitsa

18 “Yehova adzalamula

19 Akavalo a Farao, magaleta ndi oyendetsa akavalo atalowa mʼnyanja, Yehova anawabwezera madziwo mʼnyanja ndi kuwamiza, koma Aisraeli anawoloka nyanjayo powuma.

20 Ndipo Miriamu mneneri wamkazi, mlongo wa Aaroni anatenga zoyimbira ndipo akazi onse anamutsatira pambuyo, akuyimba ndi zoyimbira ndi kuvina.

21 Miriamu anawayimbira nyimbo iyi:

22 Ndipo Mose anatsogolera Israeli kuchoka ku nyanja yofiira ndi kupita ku chipululu cha Suri. Anayenda mʼchipululu masiku atatu wosapeza madzi.

23 Ndipo anafika ku Mara. Koma sanathe kumwa madzi akumeneko chifukwa anali owawa. (Ndi chifukwa chake malowo amatchedwa Mara).

24 Tsono anthu aja anadandaulira Mose ndi kumufunsa kuti, “Kodi tikumwa chiyani?”

25 Ndipo Mose anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anamuonetsa kamtengo. Iye anakaponya mʼmadzimo ndipo madzi anakhala abwino.

26 Yehova anati, “Ngati inu mudzamvetsa bwino mawu anga, kuchita zolungama, kumvera malamulo anga ndi kusamalitsa zimene ndikukuwuzani ndiye kuti Ine sindidzayika pa inu matenda amene ndinayika pa anthu a ku Igupto popeza ndine Yehova amene ndimakuchiritsani.”

27 Kenaka anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa makumi asanu ndi awiri, ndipo anamanga misasa yawo kumeneko pafupi ndi madzi.

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado