1 Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:
2 Ndipo ndinanena kuti akufa,
3 Koma wopambana onsewa
4 Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
5 Chitsiru chimangoti manja ake lobodo
6 Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,
7 Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:
8 Panali munthu amene anali yekhayekha;
9 Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,
10 Ngati winayo agwa,
11 Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.
12 Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,
13 Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo.
14 Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo.
15 Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu.
16 Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.