1 Crônicas 16

NYA

1 Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.

2 Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.

3 Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.

4 Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.

5 Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,

6 ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.

7 Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:

8 Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

9 Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando;

10 Nyadirani dzina lake loyera;

11 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita,

13 inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake,

14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

15 Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse,

16 pangano limene anachita ndi Abrahamu,

17 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo,

18 “Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani

19 Ali anthu owerengeka,

20 iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina,

21 Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze;

22 “Musakhudze odzozedwa anga;

23 Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi;

24 Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse,

25 Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

26 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake,

27 Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake;

28 Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina,

29 perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake.

30 Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi!

31 Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere;

32 Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

33 Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba,

34 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino;

35 Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu,

36 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli,

37 Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.

38 Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.

39 Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni

40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.

41 Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”

42 Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.

43 Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

Ler em outra tradução

Comparar lado a lado